Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Amumanga atanamiza anthu kuti amachulukitsa ndalama m’matsenga

Apolisi ku Limbe munzinda wa Blantyre amanga Rodrick Kaliwo wazaka 28 pomuganizira kuti wakhala akubera anthu powanamiza kuti amachulukitsa ndalama m’matsenga.

Kaliwo anamangidwaponso pamulandu ngati womwewu.

Ofalitsankhani wapolisi ku Limbe, Aubrey Singanyama, wati Kaliwo anatenga ndalama yokwana K60,000 kwa munthu wina wa bizinesi pomunamiza kuti adzayichulukitsa kukwana K900,000 mmaola awiri okha.

Zitakanika, mkuluyu anauza munthu wabizinesiyo kuti akatenge dothi la mtumbira wa manda omwe angokwiliridwa kumene, zomwe zinamudabwitsa kenako anakanena kupolisi.

Apolisi atafika kunyumba kwa Kaliwo, anapeza zinthu zosiyanasiyana zomwe amanamizira anthu kuti iyeyo ndi sing’anga.

Related posts

ESCOM delegation in Mozambique for Inter-connection power project tour

Romeo Umali

‘Kanema wa Belinda alimbikitsa atsikana’

Romeo Umali

Malawi ranks high in Esophageal Cancer

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.