Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Kale Langa yagwedeza Kaning’ina

Gulu lovina dansi pa pologalamu yapa wailesi ya Kale Langa imene imauluka pa MBC Radio one yasonkhana mu mzinda wa Mzuzu kumene akuvina dansiyo.

Mkonzi komanso muulutsi wa Pologalamuyo Sol Rasheed wati ndi okondwa kuti wachititsa Pologalamuyo live mu Mzinda wa Mzuzu kumenenso akuti wakumana ndi anthu amene amangowamva akamalemba kalata zawo pa Wailesi.

Anthuwo asangalala ndi Nyimbo za Simanjemanje komanso Kanindo zimene awonetsa luso lawo mmene amkachitira kalero popalasa fumbi mu dansi yobetcha imene amkavina mu nthawi yawo.

Wolemba: Hassan Phiri

Related posts

Boma layamikira ntchito za NASCENT Solutions polimbikitsa maphunziro

Alinafe Mlamba

Mavenda aku Nsungwi asonkhana ku High Court

Mayeso Chikhadzula

Airtel Top 8 iyamba pa 14 September

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.