Malawi Broadcasting Corporation
Crime Development Local Local News Nkhani

Ukayidi wa zaka zitatu ataba ng’ombe ya Eid

Khothi la Midima ku Limbe mu mzinda wa Blantyre lagamula kuti a Chikondi Maluwa, 23, akagwire ukayidi kwa zaka zitatu ataba ng’ombe ya anthu ena omwe anakonza kuti adzayiphe pa chikondwelero cha Eid ya 2025.

Ofalitsankhani pa Polisi ya Limbe, a Aubrey Singanyama, ati a Maluwa anaba ng’ombeyo ku Mpingwe mu mzinda omwewu.

A Singanyama ati mu bwalo la milandu, a Malawa anapempha kuti alandire chilango chofewa chifukwa sanavute kuvomereza mlanduwu.

Koma oweluza milandu anaperekabe zaka zitatuzo pofuna kupereka phunziro kwa ena amene akhoza kuchita zomwezi.

Chikondi Maluwa ndi wa m’mudzi wa Tsoka, m’dera la mfumu yayikulu Thomas m’boma la Thyolo.

 

Related posts

Researchers, policy makers urged to strengthen collaboration

Romeo Umali

Mpulula displeased with Tigers’ performance in first round of TNM Super League

MBC Online

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.