Malawi Broadcasting Corporation
Development Health Local News Nkhani

Achinyamata awapempha kuti athandize boma pa chitukuko

Bungwe la Chiwalo Youth Network lalangiza achinyamata a m’boma la Phalombe kuti athandize kulimbikitsa ukhondo m’makomo mwawo komanso m’malo a boma monga ku Polisi ndi ku chipatala.

Wapampando wa bungweli, a Patrick Makwale, ndi amene ananena izi pamene achinyamata ena amagwira ntchito yosesa pa chipatala cha boma cha Nambazo komanso Polisi ya Nambazo m’bomalo.

A Makwale anati ndi okondwa poona kuti achinyamata ambiri ku Phalombe akuonetsa chidwi pa ntchiito za chitukuko, potukula miyoyo yawo komanso ntchito za boma.

 

Related posts

People hoping to ‘beat the heat’ on polling day

Steve Dakalira

Three arrested in K22 million soybean theft

Romeo Umali

SOUTH-WEST POLICE DRILL PRIMARY STUDENTS ON ROAD SAFETY

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.