Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Sports Sports

Mtsogoleri wa FIFA akapepesa maliro a Dr Chilima

Mtsogoleri wa bungwe loyang’anira masewero a mpira wa miyendo padziko lonse la pansi la FIFA, a Gianni Infantino, akuyembekezeka kupepesa mwapadera ku banja la malemu Dr Saulos Chilima amene anali wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino.

Iwo akapepesanso kwa mtsogoleri wa dziko lino, Dr Lazarus Chakwera.

A Infantino afika m’dziko muno lachiwiri madzulo kudzera pa bwalo la ndege la Kamuzu mu mzinda wa Lilongwe pamene analandiridwa ndi mtsogoleri oyendetsa masewero a mpira wa miyendo m’dziko muno, a Fleetwood Haiya.

Koma a Infantino ayimitsa kaye dongosolo limene anakonza kuti ayambepo ntchito yoyendera masewero a mpira wa miyendo kaamba ka chisoni chomwe chakuta dziko la Malawi.

 

 

Related posts

FAO reaffirms commitment to digital rural agriculture transformation

McDonald Chiwayula

Universities urged to support MW2063 vision

Mayeso Chikhadzula

PROPHET MILWARD APEREKA THANDIZO LA K15 MILION KWA ANA A MASIYE

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.