Malawi Broadcasting Corporation
Development Health Local Local News

Tithandizane kulimbana ndi khansa ya chiberekero — Chiponda

Nduna yazaumoyo, a Khumbize Kandodo Chiponda, yatsindika kufunika kogwirana manja pa ntchito yolimbana ndi khansa ya khomo la chiberekero m’dziko muno.

Ndunayi yayakhula izi ku Lilongwe pa msonkhano okambira za matenda a khansa yokhudza khomo la chiberekero.

A Chiponda ati ndi zodandaulitsa kuti amayi oposa 3,000 pa chaka m’dziko muno akumwalira kamba ka nthendayi.

A Chiponda anaonjezera kuti unduna wa zaumoyo uonetsetsa kuti atsikana azaka za pakati pa 9 ndi 14 akulandira katemera wa HPV, yemwe amateteza ku nkhansayi kuonetsetsa kuti malo oyezera khansa ya khomo la chiberekero adzipezeka m’zipatala zonse za m’dziko muno.

Related posts

Maranatha Academy honours top-performing Form 4 students

McDonald Chiwayula

Walipira chindapusa chifukwa chonyoza wodwala AIDS

Romeo Umali

MALAWI BROADCASTING CORPORATION EXECUTIVE MANAGEMENT PLACEMENT: DIRECTOR OF HUMAN RESOURCE AND ADMINISTRATION

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.