Malawi Broadcasting Corporation
Development Health Local Local News

Tithandizane kulimbana ndi khansa ya chiberekero — Chiponda

Nduna yazaumoyo, a Khumbize Kandodo Chiponda, yatsindika kufunika kogwirana manja pa ntchito yolimbana ndi khansa ya khomo la chiberekero m’dziko muno.

Ndunayi yayakhula izi ku Lilongwe pa msonkhano okambira za matenda a khansa yokhudza khomo la chiberekero.

A Chiponda ati ndi zodandaulitsa kuti amayi oposa 3,000 pa chaka m’dziko muno akumwalira kamba ka nthendayi.

A Chiponda anaonjezera kuti unduna wa zaumoyo uonetsetsa kuti atsikana azaka za pakati pa 9 ndi 14 akulandira katemera wa HPV, yemwe amateteza ku nkhansayi kuonetsetsa kuti malo oyezera khansa ya khomo la chiberekero adzipezeka m’zipatala zonse za m’dziko muno.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

BAM condoles with Chakwera

McDonald Chiwayula

Chithyola calls on legislators to provide oversight role on budget

McDonald Chiwayula

NETP crucial for public information amidst disasters — MACRA

Madalitso Mhango
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.