Malawi Broadcasting Corporation
Development Health Local Local News

Tithandizane kulimbana ndi khansa ya chiberekero — Chiponda

Nduna yazaumoyo, a Khumbize Kandodo Chiponda, yatsindika kufunika kogwirana manja pa ntchito yolimbana ndi khansa ya khomo la chiberekero m’dziko muno.

Ndunayi yayakhula izi ku Lilongwe pa msonkhano okambira za matenda a khansa yokhudza khomo la chiberekero.

A Chiponda ati ndi zodandaulitsa kuti amayi oposa 3,000 pa chaka m’dziko muno akumwalira kamba ka nthendayi.

A Chiponda anaonjezera kuti unduna wa zaumoyo uonetsetsa kuti atsikana azaka za pakati pa 9 ndi 14 akulandira katemera wa HPV, yemwe amateteza ku nkhansayi kuonetsetsa kuti malo oyezera khansa ya khomo la chiberekero adzipezeka m’zipatala zonse za m’dziko muno.

Related posts

Controlling Officers urged to be exemplary

Rabson Kondowe

LL WAREHOUSE ROBBERY SUSPECT, ACCOMPLICE NABBED

Romeo Umali

20,000 plus men get circumcised in a quarter

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.