Nduna yazaumoyo, a Khumbize Kandodo Chiponda, yatsindika kufunika kogwirana manja pa ntchito yolimbana ndi khansa ya khomo la chiberekero m’dziko muno.
Ndunayi yayakhula izi ku Lilongwe pa msonkhano okambira za matenda a khansa yokhudza khomo la chiberekero.
A Chiponda ati ndi zodandaulitsa kuti amayi oposa 3,000 pa chaka m’dziko muno akumwalira kamba ka nthendayi.
A Chiponda anaonjezera kuti unduna wa zaumoyo uonetsetsa kuti atsikana azaka za pakati pa 9 ndi 14 akulandira katemera wa HPV, yemwe amateteza ku nkhansayi kuonetsetsa kuti malo oyezera khansa ya khomo la chiberekero adzipezeka m’zipatala zonse za m’dziko muno.