Malawi Broadcasting Corporation
News Nkhani

Adzudzula aphungu kamba kosapereka ulemu kwa Sipikala

Mmodzi mwa akuluakulu a chipani cha MCP ku nyumba ya malamulo,  a Ulemu Chilapondwa, adzudzula aphungu anyumba ya malamulo kamba ka khalidwe losapereka ulemu kwa Sipikala wa nyumba ya malamulo a Catherine Gotani Hara.

A chilapondwa, omwe ndi phungu wadera la Ntchisi South, anadandaula kuti atatulutsidwa mnyumbayi lachitatu sabata yatha, phungu wadera la Rumphi East, a Kamlepo Kalua, anakalankhula mawu onyoza sipika wanyumbayi pa masamba amchezo.

Poyankhapo pankhaniyi, mtsogoleri wazokambirana mnyumba ya malamulo, a Richard Chimwendo Banda, adandaula komanso kudzudzula  khalidwe limene adadonyeza a Kalua, yemwe akuti adanyoza mayi Catherine Gotani Hara polankhula ndi atolankhani sabata yatha.

Wachiwiri kwa sipika wanyumba yamalamulo, a Madalitso Kazombo, anatsindika kufunika kopeleka ulemu kwa mtsogoleri wanyumbayi yemwe ndi sipikala, ponena kuti malamulo a nyumbayi amafotokoza momveka bwino pa nkhani ya ulemu kwa atsogoleri.

Related posts

Govt wants to strengthen health sector

Romeo Umali

Alimi apempha Dr Chakwera kuti awathandize kupeza misika mosavuta

Mayeso Chikhadzula

Airtel hikes cost of bundles

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.