Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Tisunge bata, mtendere — Inkosi ya Makosi Goman V

Inkosi ya Makosi Gomani V ya m’boma la Ntcheu yati ili ndi chisoni chachikulu kaamba ka imfa ya Impi Bhiyeni Dr Saulos Chilima.

Inkosiyi yati Dr. Chilima anali mlangizi wa chingoni amene amamukonda, ndipo anali olimbikira, odzipereka ndi olimbikitsa chikhalidwe komanso odzipereka ku mpingo.

Iwo anayamikiranso khwimbi la anthu amene akupereka ulemu wawo otsiriza kwa malemu Dr. Chilima.

Koma iwo anati ngakhale aMalawi ali pa chisoni chachikulu, akuyenera kulimbikitsa mtendere.

Inkosi Ya Makosi Gomani yalangizanso aMalawi kuchita ndale zokomera dziko lonse.

Related posts

Avokado ayimba ndi Ndirande Anglican Voices, Great Angels

Romeo Umali

All set for Top Product Awards 2024

McDonald Chiwayula

Medina Stars yatenga chikho cha Zikhale ku Nkhata Bay

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.