Malawi Broadcasting Corporation
Agriculture Local Local News Nkhani

Zokonzekera gawo lachiwiri lokonza sikimu ya Mlambe zili mchimake

Alimi omwe akuchita nawo ulimi wa mthilira wa minda ikuluikulu pa sikimu ya Mlambe Irrigation ku Mangochi, ayamikira bungwe la Green Belt Authority (GBA) kaamba kachidwi chomwe bungweli likuonetsa polimbikitsa ntchito za sikimuyi kuti zipindulire alimi ochuluka.

Wapampando wa gulu la alimiwa, Phillip Mkwela, alankhula izi ku Mangochi pamene bungwe la GBA limapereka ntchito ya gawo lachiwiri lokonzanso sikimuyi kwa akuluakulu a kampani ya Eistein Construction.

Kampani yatsopanoyi ikuyembekezeka kukonza malo ochuluka mahekitala 352 mugawo lachiwiri la ntchitoyi.

A Mkwera ati gawo lachiwiri la ntchitoyi likupereka chiyembekezo chachikulu choti alimiwa adzipeza phindu lochuluka.

M’modzi mwa akuluakulu ku bungwe la GBA, a Synoden Kautsi, ati mwazina, kampani ya Eistein ikuyembekezeka kukonza ngalande zina zodutsa madzi, kuika magetsi oyendera mphamvu ya dzuwa, kupala ndi kukonza malo ochitira ulimi.

Malinga ndi a Kautsi, ntchitoyi yomwe ndi ya ndalama zokwana K21 billion, ikuyembekezeka kugwiridwa kwa miyezi isanu ndi inayi.

Mugawo loyamba, bungwe la GBA linakonza malo a ulimi okwana ma hekitala 48 pomwe alimi akolorapo chimanga chomwe analima.

Olemba: Owen Mavula

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Tipereke mpata kwa ena opata mphoto – Mandota

Emmanuel Chikonso

Malawi seeks to boost domestic health funding as donor support wanes

Doreen Sonani

Tifikira a Malawi  onse omwe akuvutika ndi njala

Eunice Ndhlovu
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.