Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Religion

‘Pitirizani kukhala chitsanzo chabwino kudzera m’chisilamu’

Wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino, Dr Michael Usi, walimbikitsa anthu achipembedzo cha chisilamu kuti apitirize kukhala chitsanzo chabwino pa ntchito yolimbikitsa chikondi komanso kulolerana kudzera mu chiphunzitso cha chisilamu.

Dr Usi anena izi pa bwalo la Kasolo m’boma la Mangochi pamwambo wa mapemphero komanso chikondwelero cha Eid.

Iwo anati boma limayamika ntchito yomwe achipembedzo cha chisilamu amagwira polimbikitsa chikondi, umodzi komanso kugwira ntchito za chifundo.

“Mupitirize kukhala chitsanzo chabwino ndipo pemphelerani mtendere m’dziko muno pamene tikuyandikira chisankho pa 16 September chaka chino,” Dr Usi anatero.

Wapampando wa komiti yomwe inakonza mwambowu, Sheikh Ahmad Hussein, analonjeza kuti apitiriza kugwira ntchito limodzi ndi boma.

Olemba: Owen Mavula

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

‘Kabambe’s economic vision wanting’

MBC Online

Chakwera attend Sub-region Conference of Bishops

Beatrice Mwape

Saidi calls for strict adherence to austerity measures

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.