Malawi Broadcasting Corporation
Local News

Wapolisi wafa pomwe amalimbana ndi mbava

Apolisi m’dziko muno atsimikiza za imfa ya wapolisi mzawo Petros Mhango yemwe amagwira ntchito pa polisi ya Soche ku Blantyre.

Ofalitsankhani zapolisi m’dziko muno, a Peter Kalaya, wati a Mhango afa wapolisi mzawo atawaombera mwangozi pomwe amalimbana ndi mbava ku Chileka mu mzinda womwewo wa Blantyre.

A Kalaya ati apolisi anamvetsedwa kuti anthu ena akonza zokaba kunyumba kwa munthu wina ku Chileka ndipo anathamangira ku maloko komwe anayamba kuwomberana ndi mbavazo.

Mwatsoka, wapolisi wina anaombera a Mhango omwe anatsimikizika kuti afa atafika pachipatala chachikulu cha Queen Elizabeth Central Hospital.

Pakuwomberanako, apolisi awombera ndikupha mbava ziwiri pomwe zina zinathawa.

Related posts

Traders urged to accept smaller Kwacha denominations

MBC Online

Illovo ithandiza okhudzidwa ndi kusefukira kwa madzi ku Nkhotakota

Romeo Umali

VETERAN POLITICIAN MWAMBUNGU DIES

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.