Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Politics

UTM ilingalire mozama — Mwakasungula

Mmodzi mwa akatswiri pa nkhani za utsogoleri ndi ufulu wachibadwidwe, a Undule Mwakasungula, wati ganizo la chipani cha UTM lofuna kutuluka mu mgwirizano wa Tonse lachitika pa nthawi yolakwika ndipo litha kusokoneza tsogolo lachipanichi.

Mu chikalata chomwe atulutsa, Mwakasungula ati chipanichi chikanachilimika posankha mtsogoleri watsopano komanso kupeza njira zina zokonzera mavuto awo mu mgwirizano wa Tonse.

Iwo ati ganizoli lili ndi kuthekera kogawa chipanichi.

Iwo ati utsogoleri wa Malemu Dr Saulos Chilima unali olunzanitsa anthu otsatira chipanichi mokomera chitukuko cha dziko lino.

Malinga ndi a Mwakasungula, chipanichi chisokonekera ngati sichiyenda mosamala ndikugumula maziko amene malemu Dr Chilima anawavutikira kumanga.

Olemba: Blessings Cheleuka

Related posts

Govt pledges completion of 12,500 security houses

MBC Online

Beneficiaries in Zomba want climate smart programme to continue

Alinafe Mlamba

Aphana chifukwa cha chibwenzi

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.