Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Politics

UTM ilingalire mozama — Mwakasungula

Mmodzi mwa akatswiri pa nkhani za utsogoleri ndi ufulu wachibadwidwe, a Undule Mwakasungula, wati ganizo la chipani cha UTM lofuna kutuluka mu mgwirizano wa Tonse lachitika pa nthawi yolakwika ndipo litha kusokoneza tsogolo lachipanichi.

Mu chikalata chomwe atulutsa, Mwakasungula ati chipanichi chikanachilimika posankha mtsogoleri watsopano komanso kupeza njira zina zokonzera mavuto awo mu mgwirizano wa Tonse.

Iwo ati ganizoli lili ndi kuthekera kogawa chipanichi.

Iwo ati utsogoleri wa Malemu Dr Saulos Chilima unali olunzanitsa anthu otsatira chipanichi mokomera chitukuko cha dziko lino.

Malinga ndi a Mwakasungula, chipanichi chisokonekera ngati sichiyenda mosamala ndikugumula maziko amene malemu Dr Chilima anawavutikira kumanga.

Olemba: Blessings Cheleuka

Related posts

EXPERTS DELIBERATE ENVIRONMENTAL HEALTH CHALLENGES

McDonald Chiwayula

Zikhale urges Kasungu residents to register for 2025 elections

Romeo Umali

Dzaomboleni galimoto zanu, atero a MRA

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.