Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Unduna waza umoyo ulitcheru pothana ndi kufala kwa matenda a kolera – Chikumbe

Unduna waza umoyo wati walandira katemera wa matenda a cholera 720,185 wa mkamwa kuchokera ku bungwe laza umoyo pa dziko la World Health Organization (WHO).

Mneneri ku unduna waza umoyo, a Adrian Chikumbe, anena zimenezi pomwe zadziwika kuti anthu ena m’maboma a Chitipa, Karonga, Balaka komanso Machinga apezeka ndi matenda wotsekula m’mimba a kolera.

A Chikumbe ati akugwira limodzi ntchito ndi ma unduna osiyanasiyana ndi mabubgwe okhudzidwa pofuna kudziwitsa anthu momwe angalimbanilane ndi matendawa.

Malinga ndi a Chikumbe, katemera amene alandira amupereka m’maboma onse omwe mwabuka matenda a kolera.

Related posts

‎ Govt, CAMFED seek to boost youth development

Rabson Kondowe

Bungwe la MEC layamba kuonkhetsera zotsatira za chisankho kumsonkhano waukulu wachipani cha DPP

Rabson Kondowe

ACB drills council on Corruption Risk Assessment

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.