Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Unduna waza umoyo ulitcheru pothana ndi kufala kwa matenda a kolera – Chikumbe

Unduna waza umoyo wati walandira katemera wa matenda a cholera 720,185 wa mkamwa kuchokera ku bungwe laza umoyo pa dziko la World Health Organization (WHO).

Mneneri ku unduna waza umoyo, a Adrian Chikumbe, anena zimenezi pomwe zadziwika kuti anthu ena m’maboma a Chitipa, Karonga, Balaka komanso Machinga apezeka ndi matenda wotsekula m’mimba a kolera.

A Chikumbe ati akugwira limodzi ntchito ndi ma unduna osiyanasiyana ndi mabubgwe okhudzidwa pofuna kudziwitsa anthu momwe angalimbanilane ndi matendawa.

Malinga ndi a Chikumbe, katemera amene alandira amupereka m’maboma onse omwe mwabuka matenda a kolera.

Related posts

President Chakwera akayendera ntchito zachitukuko kumpoto

Rabson Kondowe

I will not resign — Mtalimanja

Romeo Umali

Activists push for Reusable Sanitary Pads to combat period poverty

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.