Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

‘Ubale wa dziko la China ulimbikitse Malawi pa ntchito zamalonda’

Sipikala wanyumba yamalamulo a Catherine Gotani Hara ati dziko lino litengerepo mwayi paubale omwe ulinawo ndi dziko la China popititsa patsogolo ntchito zamalonda.

A Hara anena izi ku Lilongwe kutsatira kubwera kwa wachiwiri wa sipikala wa nyumba ya malamulo yadziko la China, a Cai Dafeng.

Malinga ndi a Hara, nyumba yamalamulo ndiyodzipereka kukonza malamulo komanso kupanga ena amene angathandizire nkhani zamalonda m’dziko muno.

Pakali pano dziko la China, mwazina, likugula fodya komanso soya m’dziko muno, zomwe a Hara ati ndizothandiza kupititsa patsogolo chuma chadziko lino.

Mwazina, a Dafeng anayendera nyumba yamalamulo yadziko lino,imene inamangidwa ndithandizo lochoka kudziko la China.

 

Related posts

‘Akabaza kalembetseni m’kaundula wa voti’

Romeo Umali

MDF, LCC sign MoU to rehabilitate Lilongwe roads

MBC Online

Fr. Mbandama tackles mental health issues among youths

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.