Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

‘Ubale wa dziko la China ulimbikitse Malawi pa ntchito zamalonda’

Sipikala wanyumba yamalamulo a Catherine Gotani Hara ati dziko lino litengerepo mwayi paubale omwe ulinawo ndi dziko la China popititsa patsogolo ntchito zamalonda.

A Hara anena izi ku Lilongwe kutsatira kubwera kwa wachiwiri wa sipikala wa nyumba ya malamulo yadziko la China, a Cai Dafeng.

Malinga ndi a Hara, nyumba yamalamulo ndiyodzipereka kukonza malamulo komanso kupanga ena amene angathandizire nkhani zamalonda m’dziko muno.

Pakali pano dziko la China, mwazina, likugula fodya komanso soya m’dziko muno, zomwe a Hara ati ndizothandiza kupititsa patsogolo chuma chadziko lino.

Mwazina, a Dafeng anayendera nyumba yamalamulo yadziko lino,imene inamangidwa ndithandizo lochoka kudziko la China.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

MDF calls for improved welfare of its retirees

Trust Ofesi

Kuchedwa kobwezeretsa ndalama zosochera kutha posachedwa

Arthur Chokhotho

Learner mentors making a difference in Mchinji Schools

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.