Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

‘Ubale wa dziko la China ulimbikitse Malawi pa ntchito zamalonda’

Sipikala wanyumba yamalamulo a Catherine Gotani Hara ati dziko lino litengerepo mwayi paubale omwe ulinawo ndi dziko la China popititsa patsogolo ntchito zamalonda.

A Hara anena izi ku Lilongwe kutsatira kubwera kwa wachiwiri wa sipikala wa nyumba ya malamulo yadziko la China, a Cai Dafeng.

Malinga ndi a Hara, nyumba yamalamulo ndiyodzipereka kukonza malamulo komanso kupanga ena amene angathandizire nkhani zamalonda m’dziko muno.

Pakali pano dziko la China, mwazina, likugula fodya komanso soya m’dziko muno, zomwe a Hara ati ndizothandiza kupititsa patsogolo chuma chadziko lino.

Mwazina, a Dafeng anayendera nyumba yamalamulo yadziko lino,imene inamangidwa ndithandizo lochoka kudziko la China.

 

Related posts

US eager to aid Malawi

Rabson Kondowe

Castel Malawi contributes K10 million to Presidential Charity Golf Initiative

Rabson Kondowe

Women, youths urged to lead in peace building

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.