Malawi Broadcasting Corporation
Crime Development Local Local News Nkhani

Tsogolo la mlandu wa a Mbedza lioneka masana ano

Masana ano bwalo la Magistrate mnzinda wa Lilongwe likuyembezeka kupereka chigamulo pa pempho labelo lomwe oyimira a Chiyanjano Mbedza anapereka sabata yatha.

A Mbedza anawamanga pa 22 July chaka chino powaganizira kuti ndi amene amajambula ndi kufalitsa uthenga odzetsa chisokonezo pa makina a intaneti pa tsamba lake lotchedwa Bakili Muluzi TV.

Mwa zina, ati iwo amaloza zala anthu ena kuti akukhudzidwa ndi imfa ya yemwe anali wa chiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino malemu Dr Saulos Chilima.

Lachisanu lapitalo, bwaloli linakana kupereka belo kwa a Mbedza pofuna kupereka mpata kwa apolisi kuti amalize kafukufuku wawo.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

MEC CHAIRMAN TO HOLD PUBLIC LECTURE AT MZUNI

MBC Online

Malawi observes World Tuberculosis, Leprosy Day

MBC Online

Consumers urged to use proper channels for complaints – MACRA

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.