Malawi Broadcasting Corporation
Crime Development Local Local News Nkhani

Tsogolo la mlandu wa a Mbedza lioneka masana ano

Masana ano bwalo la Magistrate mnzinda wa Lilongwe likuyembezeka kupereka chigamulo pa pempho labelo lomwe oyimira a Chiyanjano Mbedza anapereka sabata yatha.

A Mbedza anawamanga pa 22 July chaka chino powaganizira kuti ndi amene amajambula ndi kufalitsa uthenga odzetsa chisokonezo pa makina a intaneti pa tsamba lake lotchedwa Bakili Muluzi TV.

Mwa zina, ati iwo amaloza zala anthu ena kuti akukhudzidwa ndi imfa ya yemwe anali wa chiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino malemu Dr Saulos Chilima.

Lachisanu lapitalo, bwaloli linakana kupereka belo kwa a Mbedza pofuna kupereka mpata kwa apolisi kuti amalize kafukufuku wawo.

 

Related posts

SULOM charges MAFCO for Misconduct

Romeo Umali

Macra’s muuni fund empowers innovators

Romeo Umali

Malawi commemorates One Health Day

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.