Malawi Broadcasting Corporation
Entertainment Health Local News Nkhani

Temwa aveka makanda pa chipatala cha Kamuzu Central

Katswiri oyimba nyimbo za Amapiano, Temwa, wati iye ndi odzipereka kuthandiza ana osowa amene agonekedwa mu zipatala m’dziko muno.

Temwa amayankhula izi pa chipatala cha Kamuzu Central munzinda wa Lilongwe pamene amapereka zovala za mphepo ndi zina kwa ana omwe agonekedwa pa chipatalachi.

Iye wati thandizo lina lomwe ndi la ndalama zokwana K1million lachokera kwa anthu akufuna kwabwino.

Sabata ya mawa, Temwa akhala akugawa zovala kwa ophunzira osowa pa sukulu ya pulayimale ya Kalambo ku Area 25 mu mzinda wa Lilongwe.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Kalembetseni m’kaundula wa MEC kuti mudzavote — MCP

MBC Online

Dr Chakwera to visit Chitipa

MBC Online

Machinga farmers to plant 50,000 trees

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.