Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News

Awali ampatsa chilango

A Bester Awali, omwe ndi Phungu wa Chipani cha Democratic Progressive (DPP) wa dera la pakati m’boma la Zomba, awagamula kuti asadzapezeke pa nkumano wa komiti ya Nyumba ya Malamulo kwa masiku khumi (10) kaamba koponya botolo la madzi kwa a phungu a mbali ya boma nthawi imene kunali zokambirana dzulo m’nyumbayi.

Sipikala wa nyumbayi, a Catherine Gotani Hara ati poyambilira iwo adakonza chilango chokhwima zedi, koma adachepetsa popeza a Awali ndi akuluakulu ena a m’chipani cha DPP anapepesa poonetsa khalidwe loyipa.

Padakali pano, a Hara achenjeza aphungu onse kuti adzawapatsa chilango ngati adzachite m’chitidwe ochotsa ulemu wa Nyumba ya Malamulo.

#MBCDigital
#Manthu

Related posts

Last minute voter registration grips Mzimba

Romeo Umali

New livestock market brings hope to Mchinji farmers

Romeo Umali

Malawians urged to practice healthy lifestyles to combat oesophageal cancer

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.