Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani

‘Osagwiritsa ntchito imfa ya malemu Dr Chilima pa zifukwa za ndale’

Gulu lomwe likuzitcha ‘Mbadwa Zokhudzidwa’ lapempha anthu a ndale kuti asiye kugwiritsantchito imfa ya Dr Saulos Chilima pofuna kumema anthu kuti adziwakonda.

M’busa Thoko Banda, amene ndi m’modzi mwa akuluakulu a gululi amayankhula izi loweruka mu mnzinda wa Lilongwe ndipo anauza a Malawi kuti asiye kukhulupilira mabodza andale oterewa.

Mkulu winanso wa bungweli, a Billy Malata, anachenjeza a Malawi amene akufalitsa uthenga wabodza pa masamba a mchezo kuti azagamulidwa mlandu akawapeza.

A Malata analimbikitsanso chipani cha Malawi Congress (MCP) kuti chisachite ndale zonyoza.

 

Related posts

Khonsolo ya mnzinda wa Zomba ili ndi Mfumu yatsopano

Alinafe Mlamba

Anthu akukhamukira kumwambo wa Chikumbutso ku Mulanje

Romeo Umali

Chakwera commends Nkhoma Synod’s role in Malawi’s governance

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.