Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Ophunzira amenya aphunzitsi powaganizira kuti akuchita za matsenga

Apolisi ku Chikwawa akufunafuna ophunzira omwe aphwanya ofesi ya mphunzitsi wamkulu pasukulu ya pulaimale ya Mitondo m’bomalo ati poganiza kuti mphunzitsi wamkuluyo akuchita zinthu za matsenga.

Wachiwiri kwa ofalitsankhani wapolisi ku Chikwawa, Chance Mfune, wati pa 29 November, ophunzira ena pasukulupo anakomoka kaamba kakuti kunatentha kwambiri.

Koma ophunzira ena anakwiya ndi izi ndipo anatengana kupita kunyumba kwa mphunzitsi wamkuluyo poganiza kuti ndi yemwe wachititsa izi kudzera mmatsenga.

Apa chipwirikiti chinabuka mpaka anawo anamenya aphunzitsi ena awiri komanso kuba chipangizo cha mphamvu ya magetsi a dzuwa (Solar Panel) cha pasukulupo.

Related posts

Ku Mingoli Bash sikukhala oyimba akunja

Romeo Umali

FAM FINES MAFCO, BANS KAFUNDA

Romeo Umali

NICE drills volunteers ahead of 2025 elections

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.