Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Politics

Okweza dala mitengo ya katundu nthawi yawo yatha — Mumba

Nduna ya za malonda a Vitumbiko Mumba yachenjeza kuti boma sililekelera kuti aMalawi avutike ndi kukwera kwa mitengo ya zinthu kaamba ka anthu ena adyera.
A Mumba, omwenso adzayime ndi mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera pa 16 September pano, ayankhula izi m’boma la Mzimba pa misonkhano yoyimayima.
Iwo anati boma lili tchelu kuthana ndi wina aliyense yemwe akukwezera dala mitengo ya katundu pofuna kupweteka aMalawi.
Izi zikutsatira malipoti a kupezeka kwa sugar komanso cement zomwe anati anthu ena osakonda dziko lawo amabisira dala, zomwe boma la Dr Chakwera likuthana nazo.
Olemba: Grant Mhango

Related posts

‘No Doomsday, just a Blood Moon’

Romeo Umali

Ngozi zapamsewu zachuluka ku Mangochi

Rabson Kondowe

Commentators agitate for bank notes replacement to punish looters

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.