Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani Politics

‘Nyumba yamalamulo ya ana ikufunika thumba lapadera’

Komiti ya kunyumba ya malamulo yowona za chisamaliro cha anthu yati dziko lino likufunika thumba lapadera loyendetsera mikumano komanso ntchito za nyumba yamalamulo ya ana achichepere posadalira mabungwe okha.

Wapampando wa komitiyi, a Savel Kafwafwa, ndi amene anayankhula izi Lachisanu masana m’boma la Salima pa msonkhano otseka zokambirana za aphungu akunyumba ya malamulo ya ana achichepele m’bomalo.

A Kafwafwa anati izi ziyenera kudzera kunyumba yamalamulo komanso ma khonsolo a m’mizinda chifukwa kutero zithandizira kuti ntchito zamtunduwu zizipitililabe ngakhale kuti mabungwe ena atamaliza ntchito zawo.

Mlembi ku unduna oona za chisamaliro cha anthu, a Nwazi Mnthambala, anati ndi zofunikadi kuti zokambirana za ana zamtunduwu zikhazikike mu ndondomeko za boma zomwe zilipo kuti ntchitoyi ikhazikike m’dziko muno.

 

Related posts

SOS EMPOWERS 49 WOMEN WITH BUSINESS START UP SUPPORT

MBC Online

Muli ndi ufulu olowa chipani chomwe mwafuna – Brown Mpinganjira

Rabson Kondowe

MV Chambo return excites business operators

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.