Malawi Broadcasting Corporation
Entertainment Entertainment Local Local Music News Nkhani

Nyimboyi ithandize onse osweka mitima – Sife Mw

Woimba wachichepere Sife Mw, yemwe dzina lake lenileni ndi Silvia Sifenjanie Sande ndipo ali ndi zaka 21, wati nyimbo yake yatsopano ndi bvumbulutso loti litonthoze onse osweka mtima ndi mavuto osiyanasiyana monga nkhani zam’banja.

Iye wayankhula izi pamene wangotulutsa kumene kanema wa nyimbo yatsopanoyi yotchedwa ‘Make Melifa’.

Nyimboyi ikumadzafika pena poti ‘Make/Bambo a Melifa, chilichonse mukufuna mutha kutenga koma mtendere okha ndisiyireni’. Ikumafotokozanso za anthu amene banja likatha amabwereranso kudzasowetsa mtendere winayo ngakhale anayamba moyo wina.

“izi ndi nyimbo zomwe ambiri sitiyimba koma ndithu zili ndikuthekera kochilitsa onse osweka mtima. Anthu ayilandira bwino ndipo ayembekezere zazikulu kuchokera kwa ine,” Sife Mw.

Sife Mw amachokera ku Machinga kwa mfumu yaikulu Liwonde ndipo ndi mphunzitsi wakupulaimale pa sukulu ya Bolera m’boma la Mangochi.

 

Related posts

NCHE, APUMA push for closer collaboration on standards

McDonald Chiwayula

85,000 children trapped in the cruel grip of disasters in Phalombe

McDonald Chiwayula

Bullets need tactical re-calibration — Kayira

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.