Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Agwidwa ndi mankhwala oopsya ozunguza bongo

Apolisi agwira nzika yaku Niger pabwalo la ndege la KIA itabisa mankhwala woopsya kumalo wochitira chimbudzi.

Apolisi apabwaloli ati Osman Mohamed, amene ndiwa zaka makumi atatu, anapezeka ndi mankhwala wozunguza bongo a diamorphine – heroin olemera pafupifupi 1 kilogramme.

Malinga ndi ofalitsankhani wa apolisi ku KIA, a Dorrah Machila, Lachiwili Mohamed amayembekezeka kukwela ndege ya Ethiopian Airlines pa ulendo wopita m’dziko la Germany pomwe apolisi anamuchita chipikisheni.

Malinga ndi a Machila, apolisi anamupatsa madzi akumwa wotentha, zomwe zinachititsa kuti atulutse mibulu 51 ya diamorphine yomwe anaiika kumalo okhalirawo.

Malinga ndi a Machila, panopa apolisi amutsekulira Muhamed mlandu wopezeka ndi mankhwala woopsya wozunguza bongo ndipo akuyembekezeka kukaonekela kubwalo la milandu posachedwapa.

Print Friendly, PDF & Email

Author

  • Mayeso Chikhadzula joined MBC in 2006, he's an Investigative Journalist and Principal Reporter. He's also a News Anchor, Presenter, and producer.

Related posts

Pasuwa recalls Mhango for Flames AFCON qualifiers

MBC Online

‘Research, Innovation key to development’

MBC Online

Counterfeit money makers jailed

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.