Malawi Broadcasting Corporation
Development Environment Local Local News Nkhani

Namondwe sakhalapo koma mvula yamphamvu m’madera ena — MET

Nthambi yowona za nyengo yati tsopano palibe chiwopsezo choti namondwe aliyense atha kufika m’dziko muno.

Masiku apitawa, nthambiyi inalengeza kuti namondwe atha kubadwa pa nyanja ya mchere ya India lamulungu pa 10 March 2024.

Koma mu lipoti la posachedwapa, nthambiyi inatsimikiza kuti namondweyu sangakhalepo koma ngati angabadwe, mwayi ofika ku Malawi ndi ochepa zedi.

M’neneri wawo, Yobu Kachiwanda, anangoti pakadali pano anthu ayembekezere mitambo, mphepo ndi mvula m’ma boma ena akum’mwera.

A Kachiwanda anachenjezanso a Malawi kuti akhale a tcheru potsatira nkhani za nyengo.

Olemba : Blessings Cheleuka

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

M’mudzi wa Kanyenda tsopano ali ndi madzi aukhondo

Austin Fukula

Alimi aku Lilongwe asonkhanitsa K1.7 biliyoni yochitira ulimi

Emmanuel Chikonso

Community spirit shines in schoolblock project

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.