Malawi Broadcasting Corporation
Development Environment Local Local News Nkhani

Namondwe sakhalapo koma mvula yamphamvu m’madera ena — MET

Nthambi yowona za nyengo yati tsopano palibe chiwopsezo choti namondwe aliyense atha kufika m’dziko muno.

Masiku apitawa, nthambiyi inalengeza kuti namondwe atha kubadwa pa nyanja ya mchere ya India lamulungu pa 10 March 2024.

Koma mu lipoti la posachedwapa, nthambiyi inatsimikiza kuti namondweyu sangakhalepo koma ngati angabadwe, mwayi ofika ku Malawi ndi ochepa zedi.

M’neneri wawo, Yobu Kachiwanda, anangoti pakadali pano anthu ayembekezere mitambo, mphepo ndi mvula m’ma boma ena akum’mwera.

A Kachiwanda anachenjezanso a Malawi kuti akhale a tcheru potsatira nkhani za nyengo.

Olemba : Blessings Cheleuka

Related posts

Chakwera holds successful bilateral talks with UAE leadership

Romeo Umali

MEC for smooth elections

Romeo Umali

RBM assures Malawians of stable forex outlook, warns banks over unlawful forex transactions

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.