Malawi Broadcasting Corporation
Development Environment Local Local News Nkhani

Namondwe sakhalapo koma mvula yamphamvu m’madera ena — MET

Nthambi yowona za nyengo yati tsopano palibe chiwopsezo choti namondwe aliyense atha kufika m’dziko muno.

Masiku apitawa, nthambiyi inalengeza kuti namondwe atha kubadwa pa nyanja ya mchere ya India lamulungu pa 10 March 2024.

Koma mu lipoti la posachedwapa, nthambiyi inatsimikiza kuti namondweyu sangakhalepo koma ngati angabadwe, mwayi ofika ku Malawi ndi ochepa zedi.

M’neneri wawo, Yobu Kachiwanda, anangoti pakadali pano anthu ayembekezere mitambo, mphepo ndi mvula m’ma boma ena akum’mwera.

A Kachiwanda anachenjezanso a Malawi kuti akhale a tcheru potsatira nkhani za nyengo.

Olemba : Blessings Cheleuka

Related posts

President Chakwera wakhazikiska Committee ya nduna kwendeska nyifwa ya Chilima

MBC Online

Bandera ali mchitokosi pomuganizira kuti anazembetsa mtsikana wachichepere

Rabson Kondowe

SUSU IN MALAWI

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.