Malawi Broadcasting Corporation
Development Environment Local Local News Nkhani

Namondwe Filipo alibe chiopsezo ku Malawi, atero azanyengo

Nthambi yoona za nyengo m’dziko muno yatsimikiza kuti namondwe Filipo safika m’dziko muno.

Nthambiyi yati namondweyu akuyenda mobwelera ku nyanja ya mchere ya India, komwe ndi kotalikirana ndi malo okhala anthu.

M’mbuyomu, iwo adaalengeza kuti chiopsezo cha namondweyu ndi chochepa koma mpweya opepuka pa nyanja ya mchere ulimbikitsa kugwa kwa mvula m’madera ambiri m’chigawo cha kum’mwera kuyambira Lamulungu mpakana lero Lachitatu.

Ngakhale zili chomwechi, nthambiyi idaikiratu zipangizo zothandiza kupulumutsa anthu ngati ngoziyi ingachitike, mogwirizana ndi a Red Cross, asilikali a Malawi Defence Force ndi a Marine Department.

Related posts

SAFER INTERNET DAY COMMEMORATED

MBC Online

Bungwe la SFFRFM lati zokonzekera AIP zili m’chimake

Romeo Umali

Malawi urged to expedite National Migration Policy

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.