Malawi Broadcasting Corporation
International

Mulungu adalitse Iran komanso Israel — Trump

Mtsogoleri wa dziko la America, a Donald Trump, ayamikira mayiko a Israel ndi Iran kaamba koonetsa chidwi chothetsa nkhondo, malinga ndi nyumba youlutsa mawu ya BBC.

Izi zilichomwechi pamene dziko la Iran linaponya mizinga kumalo a asilikali a America m’dziko la Qatar ngati kubwezera zimene dziko la America ndi Israel anachita posakaza malo a nuclear ku Iran.

Pakadalipano, Israel yavomera kuleka kumenya nkhondo ndi Iran.

M’mawu ake, nduna yoona nkhani za kunja kwa dziko la Iran, a Seyed Araghchi, ati dziko lawo lichita chimodzimodzi ngati Israel itasiya kuchitira chiwembu dziko lawo.

Olemba: Telson Magombo

Related posts

Tanzanian President calls for peace as Mozambique awaits election results

Rabson Kondowe

Carbon as a new cash crop: How Malawi is turning trees into climate assets

McDonald Chiwayula

Africa rallies for self-reliance in health at CPHIA 2025

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.