Malawi Broadcasting Corporation
International

Mulungu adalitse Iran komanso Israel — Trump

Mtsogoleri wa dziko la America, a Donald Trump, ayamikira mayiko a Israel ndi Iran kaamba koonetsa chidwi chothetsa nkhondo, malinga ndi nyumba youlutsa mawu ya BBC.

Izi zilichomwechi pamene dziko la Iran linaponya mizinga kumalo a asilikali a America m’dziko la Qatar ngati kubwezera zimene dziko la America ndi Israel anachita posakaza malo a nuclear ku Iran.

Pakadalipano, Israel yavomera kuleka kumenya nkhondo ndi Iran.

M’mawu ake, nduna yoona nkhani za kunja kwa dziko la Iran, a Seyed Araghchi, ati dziko lawo lichita chimodzimodzi ngati Israel itasiya kuchitira chiwembu dziko lawo.

Olemba: Telson Magombo

Related posts

Malawi calls for stronger ocean conservation Efforts at African Consultation Meeting

McDonald Chiwayula

Iran President killed in Helicopter crash

Romeo Umali

Human First reaches out to 17 million people 30 years

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.