Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Mpingo wa Katolika wataya mkhristu wokhulupirika

Pamene mwambo wokhuza maliro a wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino, malemu Dr Saulos Chilima, ukupitilira ku Area 12, mtsogoleri wa bungwe la Mayi Maria mu mpingo wa Katolika mu dayosizi ya Lilongwe ndi ma dayosizi ena mdziko muno, Dr Mary Shawa, wati parishi ya St. Patrick’s komwe malemu Chilima amapemphera komanso dziko la Malawi lataya mtsogoleri yemwe anali ndi masompheya.

Dr Shawa, omwenso adapuma ngati ndi mlembi wamkulu m’boma, ati adzawakumbukira Dr Chilima ngati mkhristu wodzipereka ku ntchito ya Mulungu komanso ku dziko.

Lero ndi tsiku lachinayi dziko lino likukhuza malirowa kuchokera pomwe thupi la a Chilima ndi ena asanu ndi atatu anafa pa ngozi ya ndege.

Thupi la a Chilima likuyembekezeka kulowa m’manda lolemba sabata ya mawa kumudzi kwawo ku Ntcheu.

Related posts

Owona zaumoyo atulutsa zotsatira zonse za ‘ambuye tengeni’ mu sabata ziwiri

MBC Online

Apolisi agwira mayi atamenya ogwira ntchito mu ndege

Mayeso Chikhadzula

‘Timanga wina aliyense oyambitsa ziwawa zandale’

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.