Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Religion

Mlembi wamkulu wa Synodi akhetsa msozi ku msonkhano waukulu

Msonkhano waukulu wa mpingo wa CCAP mu Sinodi ya Livingstonia anayamba awuyimitsa kaye moderator watsopano wa sinodiyi, m’busa Jairos Kamisa, atadzudzula akuluakulu a mpingowo ‘chifukwa chosokoneza zinthu’.

Iwo anadzudzula akuluakuluwo, kuphatikizapo mlembi wamkulu wa sinodiyi, m’busa William Tembo, kuti amalowelera mu nkhani zandale, komanso amayambitsa zinthu zogawanitsa mpingo ndikuchita ziganizo mosafunsa maganizo a Moderator.

Izi zinachititsa kuti m’busa Tembo akhetse misozi pamaso pagulu lonse limene linasonkhana mu tchalichi cha Embangweni ku Mzimba.

Mmodzi mwa akuluakulu opuma a mpingowo, m’busa Mezuwa Banda, anapempha moderator watsopanoyo kuti zokambiranazo aziyimitse kaye.

Olemba: Hassan Phiri

Related posts

MW, MOZ JOINT TASKFORCE TO INVESTIGATE TRUCK DRIVER ASSAULT CASE

McDonald Chiwayula

Journalists march for sustainable environmental management

Romeo Umali

Government applauds World Bank’s youth empowerment drive in agriculture

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.