Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

MEC ionjezera masiku m’gawo loyamba la kalembera

Bungwe la Malawi Electoral Commission (MEC) lati lionjezera masiku mu kalembera wachisankho m’gawo loyamba.

Chikalata chomwe wasainira wapampando wa bungweli, Justice Annabel Mtalimanja, chati MEC yachita izi kaamba koti panalibe ogwira ntchito a bungwe la National Registration Bureau (NRB) malo olembetsera voti pamene khothi linalamula pa 25 October mwezi uno kuti malo onse olembetserawo mukhale a NRB.

MEC yati  izi sizisokoneza kalembera wagawo  lachiwiri poti bungwelo lipitilira ndi gawolo monga analengezera.

Mchikalatacho, a Mtalimanja ati MEC ikumana ndi bungwe la  NRB kuti atsatire chigamulo chomwe akhoti anapereka kuti anthu omwe akufuna kulembetsa chiphatso cha unzika athe kutero malo olembetsera voti.

 

Olemba: Austin Fukula

Related posts

Former bank teller nabbed for robbing ex-girlfriend at work

Romeo Umali

Community mourns late Shanil Dzimbiri

Rabson Kondowe

TEVETA ILIMBIKITSA ACHINYAMATA OMWE ADASIYIRA SUKULU PA NJIRA KULIMBIKIRA NTCHITO ZALUSO

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.