Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

MBC yati Kapusa anali katakwe

Mkulu wa MBC a George Kasakula ati malemu Geoffrey Kapusa anali munthu yemwe anali katakwe pantchito youlutsa mawu pa kanema komanso kuongolera tsogolo lankhani zoulutsa mawu pakanema m’dziko muno.

A Kasakula anena izi pamwambo oika m’manda a Kapusa, umene uli mkati kumudzi kwawo kwa malemwuwa.

Naye phungu wadera lakummwera kwa boma la Machinga, a Grant Ndecha, anati derali linali lokondwa kaamba kakuti linali ndi munthu yemwe achinyamata amadalira powalimbikitsa pa maphunziro kuti nawo adzakhale ndi ntchito yapamwamba.

MBC yakhala ikuthandiza a Kapusa kuyambira akudwala kufikira pano.

Related posts

Boma layamikira ntchito za NASCENT Solutions polimbikitsa maphunziro

Alinafe Mlamba

Kuchedwa kobwezeretsa ndalama zosochera kutha posachedwa

Romeo Umali

Chipatala cha Namatumi ku Thyolo achimaliza kumanga

Blessings Kanache
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.