Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

MBC yasintha matchanelo pa DSTV, GOTV

Mkulu wa Malawi Broadcasting Corporation (MBC), a George Kasakula, walengeza kuti tsopano nyumba yowulutsa mawuyi makanema ake a MBC TV komanso 2 on the Go asintha nambala za matchanelo amene amaoneka pa DSTV komanso GOTV.

A Kasakula ayankhula izi pa msonkhano wa olembankhani umene akonza limodzi ndi a Multi Choice Malawi munzinda wa Lilongwe.

Ikamafika nthawi ya 12 koloko komanso 1 koloko lero masana pa GOTV MBC TV 1 idzioneka pa nambala ya 15 ndipo MBC 2 on the Go idzioneka pa nambala 16.

Pomwe pa DSTV MBC 1 idzioneka pa nambala 268 ndipo MBC 2 on the go ikhala pa nambala 269.

A Kasakula ati MBC yachita izi pofuna kuonetsetsa kuti a Malawi akupeza uthenga komanso ma pologalamu ake mosavuta.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Chikondwelero chasefukira kwa anthu aku Mapuyu South pakukhazikitsidwa kwa ntchito ya msewu

Eunice Ndhlovu

Amabera anthu powanamiza kuti amachulukitsa ndalama

Charles Pensulo

Chakwera adzipereka pochepetsa vuto la nyumba

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.