Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

MBC yasintha matchanelo pa DSTV, GOTV

Mkulu wa Malawi Broadcasting Corporation (MBC), a George Kasakula, walengeza kuti tsopano nyumba yowulutsa mawuyi makanema ake a MBC TV komanso 2 on the Go asintha nambala za matchanelo amene amaoneka pa DSTV komanso GOTV.

A Kasakula ayankhula izi pa msonkhano wa olembankhani umene akonza limodzi ndi a Multi Choice Malawi munzinda wa Lilongwe.

Ikamafika nthawi ya 12 koloko komanso 1 koloko lero masana pa GOTV MBC TV 1 idzioneka pa nambala ya 15 ndipo MBC 2 on the Go idzioneka pa nambala 16.

Pomwe pa DSTV MBC 1 idzioneka pa nambala 268 ndipo MBC 2 on the go ikhala pa nambala 269.

A Kasakula ati MBC yachita izi pofuna kuonetsetsa kuti a Malawi akupeza uthenga komanso ma pologalamu ake mosavuta.

Related posts

Lipoti lokhudza ngozi ya ndege ku Chikangawa yatuluka

Romeo Umali

Bandera ali mchitokosi pomuganizira kuti anazembetsa mtsikana wachichepere

Rabson Kondowe

‘Osafooka maule’

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.