Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

MBC yasintha matchanelo pa DSTV, GOTV

Mkulu wa Malawi Broadcasting Corporation (MBC), a George Kasakula, walengeza kuti tsopano nyumba yowulutsa mawuyi makanema ake a MBC TV komanso 2 on the Go asintha nambala za matchanelo amene amaoneka pa DSTV komanso GOTV.

A Kasakula ayankhula izi pa msonkhano wa olembankhani umene akonza limodzi ndi a Multi Choice Malawi munzinda wa Lilongwe.

Ikamafika nthawi ya 12 koloko komanso 1 koloko lero masana pa GOTV MBC TV 1 idzioneka pa nambala ya 15 ndipo MBC 2 on the Go idzioneka pa nambala 16.

Pomwe pa DSTV MBC 1 idzioneka pa nambala 268 ndipo MBC 2 on the go ikhala pa nambala 269.

A Kasakula ati MBC yachita izi pofuna kuonetsetsa kuti a Malawi akupeza uthenga komanso ma pologalamu ake mosavuta.

Related posts

USAID yatsanzika mwapamwamba ku Fisheries

Alinafe Mlamba

Pempho layankhidwa — Aphunzitsi okhudzidwa

Romeo Umali

LUANAR itha kukwanilitsa masomphenya a Malawi 2063

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.