Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local News Nkhani

Mayi amangidwa poganiziridwa kuti wapha mwamuna wake

Apolisi ku Lilongwe amanga a Ruth Nkhoma powaganizira kuti anapha amuna awo a Misheck Bayison powakoka ndi kupotokola ziwalo zobisika kaamba kakusamvana pa ndalama yokwana K40,000 imene bambowa adamwera mowa.

Malinga ndi ofalitsankhani wa Polisiyi, a Hastings Chigalu, mayiyu ataona kuti mwamuna wake wafa, anakonza ngati kuti adadzipha yekha podzimangilira koma madotolo atapima thupi la malemuwa anatsutsa izi.

A Bayison anali a m’mudzi wa Nyenyezi kwa mfumu yayikulu Malemia m’boma la Nsanje pomwe a Nkhoma amachokera m’mudzi wa Thonyiwa kwa mfumu yayikulu Nsabwe m’boma la Thyolo.

 

Related posts

MHEN calls for strengthened eye health services

Romeo Umali

Tilitonse Foundation hosts guidance sessions for Shifting the Power Programme

McDonald Chiwayula

Illovo itolera ndalama zolimbikitsa ukhondo wa atsikana msukulu

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.