Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local News Nkhani

Mayi amangidwa poganiziridwa kuti wapha mwamuna wake

Apolisi ku Lilongwe amanga a Ruth Nkhoma powaganizira kuti anapha amuna awo a Misheck Bayison powakoka ndi kupotokola ziwalo zobisika kaamba kakusamvana pa ndalama yokwana K40,000 imene bambowa adamwera mowa.

Malinga ndi ofalitsankhani wa Polisiyi, a Hastings Chigalu, mayiyu ataona kuti mwamuna wake wafa, anakonza ngati kuti adadzipha yekha podzimangilira koma madotolo atapima thupi la malemuwa anatsutsa izi.

A Bayison anali a m’mudzi wa Nyenyezi kwa mfumu yayikulu Malemia m’boma la Nsanje pomwe a Nkhoma amachokera m’mudzi wa Thonyiwa kwa mfumu yayikulu Nsabwe m’boma la Thyolo.

 

Related posts

PDU upbeat on 50% access to electricity by 2030

Romeo Umali

GOVERNMENT MOVES ON SALIMA SUGAR COMPANY

McDonald Chiwayula

Civil thumps Hammers

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.