Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Sports Sports

Masewero a Darts m’chigawo chapakati apeza thandizo

Ligi ya masewero a Darts m’chigawo chapakati yalandira K6 million imene yachokera ku kampani yogulitsa zipangizo zaulimi ndi mankhwala ya SKM trading imenenso asayinirana nayo mgwirizano Loweruka mumzinda wa Lilongwe.

Mkulu wa za malonda ku SKM, a Asante Kagwada, anati adachita chidwi timu ya dziko lino imene inatenga mendulo ya Silver kwa kumpikisano wa maiko amu Africa m’dziko la Eswatini.

Kagwada anaonjezeranso kuti masewerowa ali ndi tsogolo lowala.

Wapampando oyendetsa ligiyi, a Hetherwick Mkudzenje, anati thandizoli liwonjezera mpikisano umene unalipo kale.

Mlembi wamkulu wa bungwe la Darts Association of Malawi, a Chikondi Maleta, anaonetsa kukondwa ndi izi ndipo anapemphanso kampani zina kuti zibwere ndi kutenganawo gawo lotukula masewerowa.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Govt assures Parliament and the nation of sugar nomalisation soon

Eunice Ndhlovu

Former President champions women’s empowerment

MBC Online

Mavenda ku 25 atseka sitolo ya m’mwenye kaamba kotsitsa mitengo

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.