Malawi Broadcasting Corporation
Development Education Local Local News Nkhani

Madam Chakwera ayamikira Press Trust potukula maphunziro

Mayi wa pfuko lino, Madam Monica Chakwera, athokoza bungwe la Press Trust pochirimika pa ntchito zotukula maphunziro m’dziko muno.
Madam Chakwera anena izi ku Chiyola mdera la Mwazisi m’boma la Rumphi pamene amatsegulira sukulu ya sekondale yoyendera ya Chiyola imene bungwe la Press Trust lamanga.
Iwo anayamikiranso bungweli pomanga sukulu zambiri m’dziko muno komanso malo ogonenera atsikana zimene ati zikutukula maphunziro.
Madam Chakwera ati kuchuluka Kwa chiwerengero cha anthu mdziko muno kwaonjezeranso vuto la kusowa kwa malo abwino ophunzirira m’sukulu zosiyanasiyana zimene ati boma silingathe kumanga pa kamodzi.
Mayi wa pfukoyi analimbikitsanso atsikana kuti asathamangire banja koma m’malo mwake aphunzire kuti adzakhale odzidalira pawokha komanso agwiritse ntchito mwayi wa sukuluyi kuti akonze tsogolo lawo.

Related posts

A Chilima adatukula kampani yathu ya Airtel — Kamoto

Mayeso Chikhadzula

Youths lead in Malawi’s green business incentive project

Romeo Umali

Two brothers nabbed over possessing Cannabis without permit

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.