Malawi Broadcasting Corporation
Agriculture Business Local Local News Nkhani

Konzekerani ulimi wa fodya — Tobacco Commission

Bungwe la Tobacco Commission lalangiza alimi a fodya m’dziko muno kuti ayambiretu ku konzekera ulimi wa fodya wa chaka cha mawa chifukwa kuzula mwachangu fodya wakale kumachepetsa matenda ndi tizilombo m’munda akabzyalamo fodya watsopano.

Ofalitsa nkhani ku bungweli, a Telephorus Chigwenembe, ndi amene anapereka langizoli pamene amazindikiritsa alimi zakufunika kozula mitengo yakale ya fodya.

A Thomson Chiwaya, amene ndi m’modzi mwa alimi a fodya, amene amakhala kwa Nyezelera m’boma la Phalombe, anati iwo anachotsa kale mitengo ya fodya ya chaka chino pokonzekera ulimi wachaka cha mawa.

Nawo a Weston Majiya, omwenso ndi mlimi wa fodya, ati ayambapo kale kusosa minda yawo ya fodya popeza alimbikitsika ndi mitengo yogulitsira fodya yomwe inaliko ku msika wa chaka chino.

 

Related posts

MRA UPBEAT TO COLLECT EXTRA K70 BN

McDonald Chiwayula

Mulanje Peaks and Rhythms Festival set for this month end

Romeo Umali

Beit Cure Hospital seeks support on children’s surgeries

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.