Malawi Broadcasting Corporation
Education Local Local News Nkhani

ISAMA ilimbikitsa maphunziro a atsikana

Bungwe la Independent Schools Association of Malawi (ISAMA) lati lipitiriza kugwira ntchito ndi mamembala ake polimbikitsa maphunziro a atsikana m’dziko muno.

Mkulu wa bungweli, a Bishop Wycliffe Chimwendo, ndi amene ananena izi pamene sukulu ya Vakusi Model High ya m’boma la Ntcheu imapereka mphoto ya ulendo wapandege ochoka ku Chileka kupita ku Lilongwe kwa ophunzira yemwe anakhoza bwino pasukuluyi m’mayeso a Form 4 apitawa, Victoria Lunduka, amene anakhoza 12 Points.

Victoria anati chinsinsi chake chakhala kulimbikira kotero walimbikitsa asungwana anzake kuti asamazikaikire.

Mphunzitsi wamkulu wa sukuluyi, a Keston Kapalamula, anati potsindika kuzipereka kwawo pa ntchito za maphunziro, atsikana ochita bwino pasukulu yawo amawapatsa ma scholarship.

Related posts

Let’s work hard and be patriotic – Usi

MBC Online

MRA achieves 100% compliance rate with Tax Stamp System

Romeo Umali

NAM interim committee confirmed

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.