Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

MANEPO idzudzula mchitidwe wa nkhanza kwa achikulire

Bungwe la Malawi Network of Older Persons’ Organizations (MANEPO) lati ndi lokhudzidwa ndi kuchuluka kwa nkhanza zomwe achikulire akukumana nazo m’dziko muno kuphatikizapo kuwaganizira kuti ndi mfiti.

Mkulu wa bungweli, a Andrew Kavala amathilirapo ndemanga pa nkhanza zomwe zachitikira  mayi Mary Laini  a zaka  87 a mmudzi mwa  Matewere kwa T/A Juma m’boma la Mulanje pomwe awanamizira kuti amamanga mvula.

A Kavala anati izi ndi kaamba ka umbuli komanso zikhulupiliro zopanda ntchito kuphatikizapo nkhani za ufiti zomwe anati ndi kuphwanya ufulu wa  achikulire m’dziko muno.

M’chikalata chomwe atulutsa a bungwe la MANEPO, apempha a polisi kuti afufuze nkhaniyi ndi kumanga onse okhudzidwa, komanso kuyika ndondomeko zothandiza kuteteza ufulu wa achikulire m’dziko muno.

A bungweli ati akutsatira ndi chidwi kuti chilungamo chiwoneke kwa mayi Laini.

 

Olemba: Grant Mhango

Related posts

Soldiers donate to Kamuzu Central Hospital

Romeo Umali

Phyzix set to invade Mzuzu

Romeo Umali

Mfumu Ngokwe yayamika magulu akufuna kwabwino

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.