Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Illovo itolera ndalama zolimbikitsa ukhondo wa atsikana msukulu

Kampani yopanga sugar ya Illovo yakonza ntchito zosiyanasiyana zofuna kutolera ndalama zothandizira ukhondo wa atsikana msukulu zina zamdziko muno.

Izi zikuchitika pansi pantchito ya Rise for Girls yomwe mwazina idzithandiza kupeza zipangizo za ukhondo zogwiritsira ntchito atsikanawa panthawi ya msambo.

Illovo yati yayika kale ndalama zokwana K100 miliyoni muntchitoyi ndipo ipitiriza kufunafunaso ndalama zina ndicholinga choti ntchitoyi ifikire atsikana ambiri.

Mmawa wa Loweluka kampaniyi inachititsa masewero a Golf ku Kasasa Golf Club m’boma la Nkhotakota pofuna kupeza ndalamazi.

Pakali pano, madyerero amgonero omwe akonza m’mbomali ngati njira imodzi yofuna kupeza ndalamazi ali mkati.

Related posts

Economists’ indaba underway, call to reshape economy

McDonald Chiwayula

Petroleum importers provides safe water to Linyangwa Health Centre

Romeo Umali

Government calls for agricultural expertise transfer

Blessings Kanache
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.