Malawi Broadcasting Corporation
Education Local News Nkhani

Fizi ilipo, koma ya mayeso palibe, Ahedi atero

Mphunzitsi wamkulu wa sukulu ya Kasitu CDSS, imene ili kudera la kumpoto m’boma la Nkhotakota, a Mixom Gama, ati ophunzira wawo Owen Nkhoma analephera kulipira ndalama ya mayeso a boma yokha a JCE yomwe ndi K19, 000.

Iwo ati sizoona kuti mnyamatayu akufunikira ndalama ya school fees, ndipo atsindika kuti iye ali pa bursary ya boma imene inayamba kumulipilira school fees kuyambira ali Form 1.

A Gama anatinso pali chiyembekezo kuti mnyamatayu abwerelanso m’kalasi m’mwezi wa September chaka chomwe chino.

Ndipo m’modzi mwa akuluakulu a khonsolo ya bomali, a McDonald Mpichi, ati aphungu akunyumba yamalamulo ndi amene amasankha ophunzira amene angapindule ndi CDF.

A Mpichi anapitiliza, “ngati ndisakulakwitsa ndalama za mayeso amayenera kulipira okha ophunzira.”

Phungu waderali, a Henry Chimunthu Banda, nawo atsindika kuti mwanayu alidi pa mndandanda wa ophunzira amene akulipiliridwa fees.

“Mwanayo akulipira fees ndi CDF. Umboni wake ndi umenewo,” a Chimunthu Banda anatero.

Umboni umene anapeleka a Chimunthu Banda.

Dzulo, m’modzi mwa anthu achifundo, a Wesley Kalenga, anapempha akufuna kwabwino, kudzera pa MBC Digital, kuti amuthandize mnyamatayu ku nkhani ya fees.

 

Related posts

Gogo Karonga laid to rest, VP and Muluzi attend funeral

Romeo Umali

National Swimming Championship kicks off in Blantyre

Rabson Kondowe

NCHE RELEASES UNIVERSITY SELECTION, MARANATHA TOPS THE LIST

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.