Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Dziperekeni pantchito – Ntemi Gwabatemi Kyungu

Ntemi Gwabatemi Kyungu yamaboma a Chitipa ndi Karonga yapempha ogwira ntchito muzipatala za m’dziko muno kukhala odzipereka pothandiza odwala komanso ndikukonda dziko lawo.

Mfumuyi yanena izi pomwe iyo ndi mafumu andodo aboma la Karonga  anakwwona ndi kucheza ndi odwala pachipatala cha Karonga pokondwelera chaka chatsopano.

Mkulu woona zaumoyo ndi ukhondo m’boma la Karonga, a David Sibale, anayamikira mfumuyi kaamba kopereka thandizoli lomwe anati labwera panthawi yake.

Pamwambowu panalinso Ntemi Kalonga, Ntemi Mwakaboko, Ntemi Mwangolera, Ntemi Mwinuka ndi amai akunyumba zachifumuzi.

Odwala omwe anawayenda ndi akuchipinda cha amuna ndipo analandira maphukusi akatundu monga sopo wochapila, wosambila, buledi ndi zakumwa za frooty.

Related posts

Musadalire kusewera ndi m’khala kale — Mapopa

Romeo Umali

K700 million chlorine tablet donation bolsters cholera readiness

Rabson Kondowe

Soche Police reduces crime by 23 percent in 2024

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.