Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Politics

Dr Usi afika mawa

Wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino, Dr Micheal Usi, afika m’dziko muno mawa atakhala nawo pa mwambo olumbilitsa mtsogoleri wa tsopano wa dziko la Mozambique, a Daniel Chapo.

A Chapo alowa m’malo mwa a Felipe Nyusi amene nthawi yawo yokhala pa udindowu inatha kutsatira pamene analamulira dzikolo maulendo awiri.

Chipani cholamula bomalo, cha FRELIMO chakhala chikulamulira dzikolo kuyambira pamene dziko la Mozambique linalandira ufulu odzilamulira m’chaka cha 1975.

Dr Usi akuyembekezeka kufika m’dziko muno nthawi ya 2:35 masana kudzera pa bwalo la Chileka munzinda wa Blantyre.

Related posts

Mbali ina ya msewu wa Chiwembe sanamange bwino — Chimwendo Banda

Romeo Umali

Three arrested in K22 million soybean theft

Romeo Umali

Man hangs himself after damaging ESCOM property

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.