Malawi Broadcasting Corporation
Entertainment Local Local Music News Nkhani

Chimbale chatsopano ndichothokoza Mulungu — Thuya

Oyimba nyimbo za uzimu, mayi busa Mary Thuya, ati chimbale chimene akutulutsa chotchedwa “Ndathokoza” ayimba pothokoza Mulungu kaamba kowachiritsa ku matenda a Covid-19.

A Thuya anena izi pokonzekera mwambo okhazikitsa chimbalechi, umene udzakhalepo Lamulungu likudzali munzinda wa Lilongwe.

Iwo ati anthu amene adzapite kumwambowu ayembekezere kukalimbikitsika kudzera ku umboni wawo.

Oyimba ena amene akaimbe nawo ndi monga Sir Norman Phiri, Favoured Martha, Alex Nkalo, Milefa Sisters komanso Maxwell Oloto.

 

Related posts

Chakwera urges UN for more support, hails cordial working relationship

Mayeso Chikhadzula

Two nabbed over K145.2 million robbery

Romeo Umali

Four nabbed for committing various crimes in Mzimba

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.