Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Nzika yaku Mozambique ayigwira itathyola ndikuba mnyumba

Apolisi m’chigawo chakummwera amanga Richard Herema  wazaka 42, yemwe kwawo ndi ku Mozambique, pomuganizira kuti iyeyo pamodzi ndi amzake,l anathyola nyumba ziwiri ndikuba ndalama zoposa K3 million komanso foni zam’manja kudera la Thornwood ku Mulanje.

Ofalitsankhani wapolisi ku Mulanje, Innocent Moses, wati Herema anali mgulu la mbava 40 zomwe zakhala zikuvutitsa mderalo.

Pakadali pano, apolisi akufufuza amzake a Herema omwe anathawa.

Herema amachokera mmudzi wa Mbizi, Mfumu yaikulu Nazombe ku Milanje m’dziko la Mozambique koma amakonza njinga zakapalasa zowonongeka kuno ku Malawi.

#MBCDigital
#Manthu

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Viral Conjunctivitis outbreak hits Mchinji

Alinafe Mlamba

Ex-MBC, MANA intern constructs child care centres

MBC Online

Ali m’chitokosi pogonana ndi mwana

Charles Pensulo
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.