Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Chikondwelero chasefukira kwa anthu aku Mapuyu South pakukhazikitsidwa kwa ntchito ya msewu

Kuli chisangalalo chokhachokha mmudzi mwa Mzonde komwe mtsogoleri wadziko lino, Dr Lazarus Chakwera, akukhazikitsa ntchito yomanga misewu, pansi pantchito ya Millennium Challenge Account.

Anthu ochuluka afika pa bwalo la Mzonde pomwe aikapo kanema yayikulu kuti akhoza kutsatira mwambo onse.

A Lettina Kalumbi a mmudzi mwa Tsabango ndi m’modzi mwa anthu mazanamazana omwe afika kudzaonelera kutsekulira kwa ntchitoyi ndipo akuti iwo ndi anzawo ochuluka ayenda makilomita oposa 5 kuchokera kwa Msundwe kudzaona kukhazikitsidwa kwa ntchitoyi, ati kuti akhale ndi umboni kuti yayambadi.

A Kalumbi akuti ndionyadira poti msewu umenewu ndiofunika pokagulitsa mbewu zawo, yomwe ndi ntchito yawo ya tsiku ndi tsiku.

Related posts

MEC, oweruza a Malawi ndi Kenya aombana mitu paza milandu ya chisankho

Romeo Umali

Health advocates push for drug theft ‘special’ court

Romeo Umali

Parliament okays K33 billion loan bill for Mangochi-Makanjira Road

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.