Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Chikondwelero chasefukira kwa anthu aku Mapuyu South pakukhazikitsidwa kwa ntchito ya msewu

Kuli chisangalalo chokhachokha mmudzi mwa Mzonde komwe mtsogoleri wadziko lino, Dr Lazarus Chakwera, akukhazikitsa ntchito yomanga misewu, pansi pantchito ya Millennium Challenge Account.

Anthu ochuluka afika pa bwalo la Mzonde pomwe aikapo kanema yayikulu kuti akhoza kutsatira mwambo onse.

A Lettina Kalumbi a mmudzi mwa Tsabango ndi m’modzi mwa anthu mazanamazana omwe afika kudzaonelera kutsekulira kwa ntchitoyi ndipo akuti iwo ndi anzawo ochuluka ayenda makilomita oposa 5 kuchokera kwa Msundwe kudzaona kukhazikitsidwa kwa ntchitoyi, ati kuti akhale ndi umboni kuti yayambadi.

A Kalumbi akuti ndionyadira poti msewu umenewu ndiofunika pokagulitsa mbewu zawo, yomwe ndi ntchito yawo ya tsiku ndi tsiku.

Related posts

CHAKWERA SECURES K32 BN FOR GOLOMOTI SOLAR POWER PLANT

MBC Online

Form One girl nabbed for stabbing her boyfriend

Rabson Kondowe

Let’s promote expressive arts in schools – JICA

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.