Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani

Chigamulo ndi mawa — Hara

Sipikala wa Nyumba ya Malamulo, a Catherine Gotani Hara, wati apereka chigamulo mawa paza mpungwepungwe umene unali m’nyumbayi akachita zokambirana ndi akuluakulu ena.

Lachinayi, a Bester Awali, omwe ndi phungu otsutsa wadera la pakati m’boma la Zomba, anaponya botolo la madzi lomwe linagwera kumbali ya Boma, zomwe zinapangitsa a Hara kunena kuti khalidweli ndi loyipa.

Izi zimachitika pamene a Joshua Malango, phungu wa pakati cha kum’mvuma kwa boma la Dedza, anapempha a Sameer Suleiman kuti achotsedwe ngati wa pampando wa komiti yoona za malimidwe kaamba ka khalidwe loyipa.

Nkhaniyi inayamba cha kum’mawa ndipo inapitilira mpaka masana, zomwe zinachititsa kuti aphungu aweruke mochedwa.

#MBCDigital
#Manthu

Related posts

MRA donates K60 million to support Cyclone Jude survivors

McDonald Chiwayula

Another BT derby awaits in FDH Bank Cup

Romeo Umali

MACRA TO INCREASE BROADBAND BY 10%

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.