Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani

Chigamulo ndi mawa — Hara

Sipikala wa Nyumba ya Malamulo, a Catherine Gotani Hara, wati apereka chigamulo mawa paza mpungwepungwe umene unali m’nyumbayi akachita zokambirana ndi akuluakulu ena.

Lachinayi, a Bester Awali, omwe ndi phungu otsutsa wadera la pakati m’boma la Zomba, anaponya botolo la madzi lomwe linagwera kumbali ya Boma, zomwe zinapangitsa a Hara kunena kuti khalidweli ndi loyipa.

Izi zimachitika pamene a Joshua Malango, phungu wa pakati cha kum’mvuma kwa boma la Dedza, anapempha a Sameer Suleiman kuti achotsedwe ngati wa pampando wa komiti yoona za malimidwe kaamba ka khalidwe loyipa.

Nkhaniyi inayamba cha kum’mawa ndipo inapitilira mpaka masana, zomwe zinachititsa kuti aphungu aweruke mochedwa.

#MBCDigital
#Manthu

Related posts

MAGU She-Wolves defend Mo626 title

Yamikani Simtowe

LWB donates K3.5 million cheque to MISA Malawi

Rabson Kondowe

Thin plastic saga takes new twist

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.