Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Chakwera alembetsa mu kaundula wa voti

Mtsogoleri wa dziko lino, Dr Lazarus Chakwera komanso mayi wa dziko lino Madam Monica Chakwera, alembetsa mu kaundula wa voti pa sukulu  ya Malembo  m’boma la Lilongwe.

Dr Chakwera ndi mai wa dziko linoyu alembetsa mu kaundulayu pomwe akuchititsa misonkhano yoimaima yomemeza anthu kuti alembetse mkaundulayu m’boma la Lilongwe.

Atalembetsa mu kaundulayu, Mtsogoleri wa dziko linoyu walimbikitsa a Malawi onse kuti atengelepo chitsanzo pokalembetsa mu kaundulayu poti ati ndi ufulu wawo ndipo  akatelo zidzawapatsa mphamvu  yodzaponya voti    pa chisankho cha chaka cha mawa.

Bungwe la MEC linatsegulira gawo lachitatu  lolembetsa mu kaundulayu  lomwenso ndi lomaliza  28 November ndipo lidzatha pa 11 December.

Related posts

Oxfam adds voice to call for aid for countries hit by hunger and flooding crisis

Rabson Kondowe

Catholics urged to be self-reliant

Romeo Umali

Four arrested for armed robbery in Nkhata Bay

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.