Malawi Broadcasting Corporation
News Nkhani

Bushiri agawa chakudya kwa okhudzidwa ndi njala ku Nkhotakota

Prophet Shepherd Bushiri wati ndi okhudzidwa ndi mavuto anjala amene akhudza anthu ambiri okhala mdera la Sub-T/A Nkhanga m’boma la Nkhotakota.

Poyankhula pamwambo ogawa chimanga kwa anthu okwana 1,300 m’deralo, mneneri wa a Bushiri, Aubrey Kusakala anati anthu am’deralo akhale ndi chiyembekezo komanso chikhulupiliro kuti Mulungu asintha nyengo zawo.

M’mawu awo, a Group Village Headman Kakopa anati thandizoli lafika munthawi yake ndipo athokoza Prophet Bushiri chifukwa cha mtima wawo wachifundo.

Ena mwa maboma amene alandira kale chimangachi ndi monga Zomba, Lilongwe, Nsanje, Thyolo, Mulanje, Ntcheu, Karonga komanso Mangochi ndipo ntchitoyi ikupitilirabe.

 

Related posts

We want a Police Unit — Dedza North West

Rabson Kondowe

Daka, Katchomoza at the helm of MRA

Rabson Kondowe

G2G vessel arrives at Nacara Port with 22 Million litres of diesel for Malawi

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.