Malawi Broadcasting Corporation
News Nkhani

Bushiri agawa chakudya kwa okhudzidwa ndi njala ku Nkhotakota

Prophet Shepherd Bushiri wati ndi okhudzidwa ndi mavuto anjala amene akhudza anthu ambiri okhala mdera la Sub-T/A Nkhanga m’boma la Nkhotakota.

Poyankhula pamwambo ogawa chimanga kwa anthu okwana 1,300 m’deralo, mneneri wa a Bushiri, Aubrey Kusakala anati anthu am’deralo akhale ndi chiyembekezo komanso chikhulupiliro kuti Mulungu asintha nyengo zawo.

M’mawu awo, a Group Village Headman Kakopa anati thandizoli lafika munthawi yake ndipo athokoza Prophet Bushiri chifukwa cha mtima wawo wachifundo.

Ena mwa maboma amene alandira kale chimangachi ndi monga Zomba, Lilongwe, Nsanje, Thyolo, Mulanje, Ntcheu, Karonga komanso Mangochi ndipo ntchitoyi ikupitilirabe.

 

Related posts

Youths urged to boost development through innovation

Rabson Kondowe

Chakwera ali pa mkumano ndi mabungwe othandiza pa ngozi zogwa mwadzidzidzi

Romeo Umali

VP to attend Human Resource Society of Malawi AGM

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.