Malawi Broadcasting Corporation
Entertainment Local Nkhani

Burning Spear wapereka mphatso ya gitala kwa President Chakwera

Katswiri oyimba nyimbo za chamba cha Reggae, Burning Spear, wapereka gitala yake imene wakhala akuyigwiritsa ntchito kwa nthawi yayitali kwa mtsogoleri wa dziko lino, Dr Lazarus Chakwera, ngati mphatso.

Lachisanu, oyimbayu anakaonekera kwa Dr Chakwera ku Kamuzu Palace munzinda wa Lilongwe ndipo anati ndi okondwa.

Mtsogoleri wa dziko linoyu anauza katswiriyu kuti wakhala akutsatira nyimbo zake kwa nthawi yaitali chifukwa ndi zolimbikitsa chilungamo, bata komanso kumenyera ufulu.

Burning Spear ayimba Loweruka lino pa bwalo la Civo munzindawu.

 

Olemba: Isaac Jali

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Namondwe Filipo alibe chiopsezo ku Malawi, atero azanyengo

Romeo Umali

BOMA LATHETSA MULANDU WA OSOKONEZA MDIPITI

Blessings Kanache

DoDMA rescues 90% of food-insecure Malawians

Beatrice Mwape
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.