Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Bungwe la MEC lalowa mu mgwirizano obwerekana katundu ndi bungwe la ECZ

Bungwe loyendesa chisankho m’dziko muno la MEC lalowa mu m’gwirizano obwerekana katundu oyendetsera chisankho ndi bungwe loyendesa chisankho la ECZ la m’dziko la Zambia.

Ngati mbali imodzi ya mgwirizanowu, MEC yabwereka majenereta 1,500 kuchokera ku ECZ kuti adzathandizire pa ntchito yakalembera wa chisankho cha chaka chamawa.

Malinga ndi chikalata chomwe atulusa a MEC, majeneretawa ndiofunika kwambiri chifukwa adzathandizira kuti ntchito yakalembera idzayende mopanda zotsamwitsa.

Bungweli lati majeneleta 1,500 wa afika m’dziko muno pa 8 September, 2024 kudzera m’boma la Mchinji.

Bungwe la MEC latinso kubwerekana katundu oyendetsera chisankho pakati pa maiko a mu SADC sizachilendo chifukwa mchaka cha 2014, dziko la Malawi linabwereka nyali komanso ma tenti kuchokera m’maiko a Zimbabwe komanso Zambia.

Ndipo mchaka cha 2020, bungwe la ECZ nalo linabwereka mageneleta 2,200 kuchokera ku bungwe la MEC omwe anagwiritsa ntchito pa chisankho cham’chaka cha 2021 cha m’dzikolo.

 

Olemba Alufisha Fischer

Related posts

Another BT derby awaits in FDH Bank Cup

Romeo Umali

Malawi, China sign $50 million deal for an Agricultural Industrial Park in Salima

Romeo Umali

Amangidwa kaamba koganiziridwa kuti adagwilirira mwana

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.